Back to Languages
Chichewa - Chapter 102
Translation by Al Haji Yusuf Muhammad Kanyamula
Verse 1
Mpikisano wosonkhanitsa chuma cha padziko wakutangwanikitsani inu
Verse 2
Mpaka pamene inu mulowa m’manda
Verse 3
Iyayi! Inu mudzadziwa
Verse 4
Kachiwiri, Iyayi! Inu mudzadziwa
Verse 5
Iyayi! Inu mukanadziwa kwenikweni
Verse 6
Ndithudi inu mudzaona moto woyaka
Verse 7
Kachiwiri inu mudzauona ndi maso anu
Verse 8
Ndipo patsiku limeneli inu mudzafunsidwa za chisangalalo chimene munali kuchita