Back to Languages

    Chichewa - Chapter 23

    Translation by Al Haji Yusuf Muhammad Kanyamula

    Verse 1

    Anthu okhulupirira ndiwo opambana

    Verse 2

    Iwo amene amadzichepetsa akamapemphera

    Verse 3

    Ndi iwo amene amalewa nkhani zabodza

    Verse 4

    Ndipo amapereka zaulere kwa anthu osauka

    Verse 5

    Ndi iwo amene amadziteteza ku chiwerewere

    Verse 6

    Kupatula kwa akazi awo kapena akapolo awo akazi, chifukwa iwo sangadzudzulidwe

    Verse 7

    Koma amene angafune zina pamwamba pa zimene tawaloleza anthu otere ndi ochimwa

    Verse 8

    Amene amakwaniritsa malonjezo ndi mapangano awo

    Verse 9

    Ndi iwo amene amasunga mapemphero awo

    Verse 10

    Amenewa ndithudi ndiwo amene adzalowa

    Verse 11

    Iwo adzalowa ku Paradiso ya pamwamba ndipo adzakhalamo mpaka kalekale

    Verse 12

    Ndithudi Ife tidapanga munthu kuchokera ku dothi labwino

    Verse 13

    Titatero tidamukonza iye kukhala dontho la umuna m’malo otetezedwa mu msana

    Verse 14

    dontho la umunali tidalipanga kukhala dontho la magazi ndipo dontho lamagazili tidalipanga kukhala m’bulu wa mnofu. Ndipo mnofu umenewu tidaukonza kukhala mafupa ndipo tidakuta mafupa ndi mnofu. Kotero tidamupanga iye kukhala chilengedwe china. odalitsa akhale Mulungu, Namalenga wabwino kwambiri mwa onse

    Verse 15

    Ndipo pambuyo pake inu nonse mudzafa

    Verse 16

    Ndipo mudzapatsidwanso moyo patsiku la kuuka kwa akufa

    Verse 17

    Ife tidalenga miyamba isanu ndi iwiri pamwamba panu ndipo kwa zolengedwa zathu. Ndipo Ife sitikhala osalabadira ayi

    Verse 18

    Ife timatumiza madzi kuchokera kumwamba m’muyeso wokwana ndipo timawalowetsa pansi pa nthaka. Ndipo Ife tili ndi mphamvu yowachotsa madziwo

    Verse 19

    Ndipo Ife timakutulutsirani mmenemo minda ya tende ndi mphesa, m’mene muli zipatso zanu zambiri zimene zina mwa izo mumadya

    Verse 20

    Mtengo umene umamera pa phiri la Sinai, umapereka mafuta ndiponso ndiwo kwa anthu

    Verse 21

    M’nyama namonso muli chizindikiro choonetsa mphamvu zathu. Inu timakumwetsani zimene zili m’mimba mwake ndipo mumadya nyama yake ndiponso mumapeza phindu lambiri

    Verse 22

    Ndipo pa izo ndi m’zombo zimene zimayenda pa nyanja, inu mumanyamulidwa

    Verse 23

    Tidamutumiza Nowa kwa anthu ake ndipo iye adati, “Tumikirani Mulungu anthu anga chifukwa mulibe mulungu wina koma Iye yekha. Kodi simungamuope Iye?”

    Verse 24

    Akuluakulu osakhulupirira a anthu ake adati, “Munthu uyu ndi wolingana ndi inu, iye ali kungodziyenereza kuti ndi wopambana pakati panu.” Mulungu akadafuna, akadatumiza angelo. Ndiponso zinthu za mtundu uwu sitidamvepo kuchokera kwa makolo athu akalekale

    Verse 25

    Ndithudi ameneyu ndi wopenga, ndipo mumuyang’anire pa kanthawi.”

    Verse 26

    Iye adati, “Ambuye! Ndithandizeni ine chifukwa iwo ali kundikana.”

    Verse 27

    Ife tidavumbulutsa chifuniro chathu kwa iye ponena kuti, “Khoma chombo chimene Ife tidzayang’anira molingana ndi chilangizo chathu. Pamene chiweruzo chathu chidza ndipo madzi asefukira kuchokera ku ng’anjo, utenge zolengedwa ziwiriziwiri, zazimuna ndi zazikazi ndiponso kuchokera kwa iwo a m’nyumba mwako kupatula okhawo amene adanenedwa kuti adzaonongeka. Usandipemphe kuti ndipulumutse iwo amene adachita zoipa chifukwa iwo adzamizidwa.”

    Verse 28

    Ndipo pamene iwe ndi iwo amene akutsata iwe mulowa m’chombo, nena, “Kuyamikidwa kukhale kwa Mulungu amene watipulumutsa ife kuchoka ku mtundu wa anthu oipa.”

    Verse 29

    Ndipo nena: “Ambuye wanga! Ndithandizeni kuti ndikafike pamalo podalitsika chifukwa Inu ndinu wabwino wa onse amene amafikitsa pamalo okocheza.”

    Verse 30

    Ndithudi mu zimenezi muli zizindikiro zooneka. Ndithudi Ife timawaika anthu m’mayesero

    Verse 31

    Potero Ife tidapanga mtundu wa anthu a tsopano pambuyo pawo

    Verse 32

    Ndipo tidatumiza kwa iwo Mtumwi wa mtundu wawo amene adati, “Tumikirani Mulungu chifukwa inu mulibe mulungu wina koma Iye yekha. Kodi simungamuope Mulungu?”

    Verse 33

    Koma akuluakulu a anthu osakhulupirira a anthu ake, amene adakana za moyo umene uli nkudza ndi amene tidawapatsa zinthu zabwino za m’moyo uno adati, “Munthu uyu ndi munthu monga inu nomwe amene akudya zimene mumadya inu ndi kumwa zimene inu mumamwa.”

    Verse 34

    “Ngati inu mumvera munthu wonga inu nomwe, ndithudi, inu mudzatayika.”

    Verse 35

    “Kodi iye ali kukuopsezani kuti pamene inu mutafa ndi kusanduka dothi ndi mafupa mudzadzuka ndi kukhalanso ndi moyo?”

    Verse 36

    “Zimene inu muli kuopsezedwa nazo zili kutali.”

    Verse 37

    “Kulibenso moyo wina koma moyo wathu wapadziko lapansi basi. Ife timafa ndi kukhala ndi moyo ndipo ife sitidzadzukanso ayi.”

    Verse 38

    “Munthu uyu ndi odziyenereza amene ali kunena za Mulungu zimene sizili zoona ayi. Ife sitidzamukhulupirira.”

    Verse 39

    Iye adati, “Ambuye! Ndithandizeni ine chifukwa iwo ali kunditsutsa.”

    Verse 40

    Iye adati, “Posachedwapa iwo adzanong’oneza bombono.”

    Verse 41

    Chilango chathu chidawapeza mwachilungamo ndipo tidawafafaniza monga zinyalala. Chionongeko kwa anthu onse ochimwa

    Verse 42

    Atapita awa tidalenganso mitundu ina ya anthu

    Verse 43

    Palibeanthuameneangafulumizitsekapenakuchedwetsa chionongeko chawo

    Verse 44

    Ndipo Ife tidatumiza Atumwi ena motsagana ndipo nthawi iliyonse Mtumwi amadza kwa iwo ndipo amamukana nati ndi wabodza. Ndipo Ife tidawaononga ena pambuyo pawo ndipo tidawapanga iwo kukhala chitsanzo cha mbiri ya anthu olakwa. Ichi chidali chionongeko cha anthu osakhulupirira

    Verse 45

    Ndipo Ife tidamutumiza Mose pamodzi ndi m’bale wake Aroni ndi zizindikiro ndiponso ulamuliro wathu

    Verse 46

    Kwa Farawo ndi nduna zake ndipo iwo adawalandira mwamwano chifukwa iwo adali anthu a chipongwe

    Verse 47

    Ndipo iwo adati, “Kodi ife tikhulupirire anthu awiri olingana ndi ife amene anthu awo ndi akapolo athu?”

    Verse 48

    Iwo adawakana iwo kotero iwo adalandira chionongeko

    Verse 49

    Ndipo Ife tidamupatsa Mose Buku la Chipangano Chakale kuti anthu ake akhoza kutsogozedwa bwino

    Verse 50

    Ife tidamupanga mwana wamwamuna wa Maria pamodzi ndi amayi ake kukhala chizindikiro kwa anthu onse ndipo tidawapatsa mnthunzi pa malo okwera ndi malo a mtendere amene anali kuthiriridwa ndi madzi a pa kasupe

    Verse 51

    Oh Atumwi! Idyani zinthu zabwino ndipo muzichita ntchito zabwino. Ndithudi Ine ndimadziwa zonse zimene mumachita

    Verse 52

    Ndithudi chipembedzo chanu ndi chimodzi ndipo Ine ndine Ambuye wanu. Kotero ndiopeni Ine

    Verse 53

    Koma anthu adagawanika m’magulu osiyanasiyana, gulu lililonse limasangalala ndi ziphunzitso zawo

    Verse 54

    Alekeni ayambe achimwa mpaka pamene imfa iwapeza

    Verse 55

    Kodi iwo amaganiza kuti popeza tawapatsa chuma ndi ana

    Verse 56

    Ndiye kuti Ife tili kuwafunira zabwino? Iyayi. Iwo sadziwa kanthu ayi

    Verse 57

    Ndithudi iwo ndi anthu amene amaopa Ambuye wawo

    Verse 58

    Amene amakhulupirira zizindikiro za Ambuye wawo

    Verse 59

    Amene sapembedza wina aliyense poonjezera pa Ambuye wawo

    Verse 60

    Amene amapereka chaulere mitima ili yoopa Ambuye wawo chifukwa chakuti adzabwerera kwa Iye

    Verse 61

    Awa ndiwo amene amapikisana wina ndi mnzake pochita zabwino ndipo amakhala oyamba pozindikira

    Verse 62

    Ife sitinyamulitsa mzimu wina uliwonse katundu amene iwo sangathe kunyamula. M’buku lathu mudalembedwa zoona zokhazokha. Ndipo palibe munthu amene adzaponderezedwa

    Verse 63

    Koma mitima ya anthu osakhulupirira siyizidziwa zimenezi ayi. Iwo ali ndi ntchito zina zoipa kupatula zimene iwo amachita

    Verse 64

    Koma pamene chilango chathu chidza pa iwo amene amakhala mu mtendere, iwo adzafuula kufuna chithandizo

    Verse 65

    Musalire tsiku la lero chifukwa inu simudzalandira chithandizo china chilichonse kuchokera kwa Ife

    Verse 66

    Chivumbulutso changa chinali kulakatulidwa kwa inu nthawi zambiri koma inu munali kuthawa ndi kuchikana mwamwano

    Verse 67

    Inu mumachinyoza usana ndi usiku uliwonse

    Verse 68

    Kodi iwo sangathe kulingalira mozama pa mawu a Mulungu kapena pali china chake chimene chidavumbulutsidwa kwa iwo chimene sichidavumbulutsidwe kwa makolo awo

    Verse 69

    Kapena iwo sadziwa kuti akukana Mtumwi wawo

    Verse 70

    Kapena iwo akuti Iye ndi wopenga? Koma iye wawabweretsera iwo onse zoonadi. Koma ambiri amakana choonadi

    Verse 71

    Kukadakhala kuti choonadi chimatsatira zofuna zawo, ndithudi, kumwamba, dziko lapansi ndi onse okhala m’menemo akadaonongeka. Ife tawapatsa chikumbutso komabe iwo safuna kumvera chikumbutsocho

    Verse 72

    Kapena iwe uli kuwapemphera mphotho? Chithandizo cha Ambuye wawo ndicho chabwino. Ndipo Iye ndiye wopereka moolowa manja kuposa onse amene amapereka

    Verse 73

    Ndithudi iwe uli kuwaitana kuti adze kunjira yoyenera

    Verse 74

    Ndithudi iwo amene amakana moyo umene uli nkudza adzakhala ali kusochera ku njira yoyenerayi

    Verse 75

    Ngati Ife tikadawalangiza chisoni chathu ndi kuwachotsera mavuto, iwo akadakhala ali kulakwabe m’njira zawo zoipa ndi kusokonezeka ndi zoipazo

    Verse 76

    Ndithudi tidawalanga kale koma iwo sadafunefune Ambuye wawo kapena kukhala odzichepetsa pamaso pake

    Verse 77

    Mpaka pamene tidzawatsekulira khomo la chilango chowawa, iwo adzakhala okhumudwa

    Verse 78

    Iye ndiye amene adakupatsani makutu, maso ndi mitima. Komabe inu simuthokoza mokwanira

    Verse 79

    Iye ndiye amene adakulengani ndi kukuchulukitsani padziko lapansi ndipo nonsenu mudzasonkhanitsidwa kudza pamaso pake

    Verse 80

    Iye ndiye amene amapereka moyo ndiponso imfa ndipo ndi Iyenso amene amasithanitsa usiku ndi usana. Kodi simungazindikire

    Verse 81

    Iwo amanena zimene anthu akale ankanena

    Verse 82

    Iwo amati, “Pamene ife tafa ndi kusanduka dothi ndi mafupa, kodi tidzadzukanso ndi kukhala ndi moyo?”

    Verse 83

    Ndithudi ife tidalonjedzedwa zimenezi kale pamodzi ndi makolo athu. Izi si zina ayi koma nkhani zabodza za anthu a makedzana

    Verse 84

    Nena, “Kodi Mwini wake wa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mmenemo ndani? Ndiuzeni ngati mumudziwa.”

    Verse 85

    Iwo adzati, “Mwini wake ndi Mulungu.” Nena, “Kodi inu simungachenjezedwe?”

    Verse 86

    Nena, “Kodi Ambuye wa miyamba isanu ndi iwiri ndiponso Mwini Ufumu ndani?”

    Verse 87

    Iwo adzati, “Mwini wake ndi Mulungu.” Nena, “Nanga kodi simungasiye kuchita zoipa?”

    Verse 88

    Nena, “Kodi ulamuliro wa zinthu zonse zili m’manja mwa yani? Kodi ndani amene amaziteteza zonse pamene Iye safuna chitetezo cha wina aliyense ngati inu mukudziwa?”

    Verse 89

    Iwo adzati, “M’manja mwa Mulungu.” Nena, “Nanga ndi chifukwa chiyani inu mwanyengedwa?”

    Verse 90

    Iyayi, Ife tawavumbulutsira choonadi. Koma onsewa ndi anthu abodza

    Verse 91

    Palibe nthawi imene Mulungu adabala mwana ndipo kulibe Mulungu wina woonjezera pa Iye. Ngati izi zikadakhala choncho, bwezi Mulungu aliyense akumatenga zolengedwa zake zokha ndi kumaziika pamwamba pa zolengedwa za Mulungu wina. Ulemerero ukhale kwa Mulungu woposa zina zilizonse

    Verse 92

    Iye amadziwa zonse zooneka ndiponso zobisika. Mulungu akhale wopambana milungu ina imene iwo amaitumikira

    Verse 93

    Nena, “Ambuye wanga! Ngati Inu mukadandionetsa chilango chimene muli kuwopseza

    Verse 94

    Ambuye wanga! Pulumutsani ndipo musandisiye ine pakati pa mtundu wa anthu oipawu.”

    Verse 95

    Ndithudi, Ife tili ndi mphamvu zoti ukhoza kuona chilango chimene tawaopseza

    Verse 96

    Dzitetezeni ndi chabwino pothamangitsa choipa. Ife tili kudziwa zonse zimene ali kukunamizirani

    Verse 97

    Ndipo iwe unene kuti, “Ambuye wanga, Ine ndili kufuna chitetezo chanu pothawa zoipa za Satana.”

    Verse 98

    “Ambuye! Ine ndili kupempha chitetezo chanu kuti asabwere kumene ndili ine.”

    Verse 99

    Mpaka pamene imfa idza kwa munthu wolakwa iye adzati, “Ambuye wanga! Bwezeni.”

    Verse 100

    “Kuti ndikachite ntchitozabwinozimenendidalepherakuchita.” Kosatheka! Amenewa ndiwo mawu chabe amene akungolankhula. Kumbuyo kwawo kudzakhala chipupa mpaka pa tsiku la kuuka kwa akufa

    Verse 101

    Ndipo pamene lipenga lidzaombedwa, pa tsiku limeneli, ubale wawo wonse udzathera pomwepo ndiponso sadzafunsana chithandizo chochokera kwa wina ndi mnzake

    Verse 102

    Aliyense amene muyeso wake udzakhala wolemera, adzapambana

    Verse 103

    Koma aliyense amene muyeso wake udzakhala wopepuka adzataya moyo wake ndipo adzakhala ku Gahena nthawi zonse

    Verse 104

    Moto udzatentha nkhope zawo ndipo izo zidzakwinyikakwinyika chifukwa chaululu

    Verse 105

    “Kodi chivumbulutso chathu sichidalakatulidwe kwa inu? Kodi simudachikane?”

    Verse 106

    Iwo adzati, “Ambuye wathu! Zilakolako zathu zidatigonjetsa ife ndipo tidali anthu osochera.”

    Verse 107

    “Ambuye wathu! tipulumutseni ife ku ichi. Ngati ife tidzabwereranso ku zoipa, ndithudi, ife tidzakhala anthu oipa kwambiri.”

    Verse 108

    Iye adzati, “Khalani mu icho mwamanyazi ndipo musandiyankhulitse Ine ayi.”

    Verse 109

    Ndithudi padali gulu la Atumiki anga amene adati, “Ambuye wathu! Ife timakhulupirira mwa inu. Tikhululukireni ndipo mutichitire chisoni. Inu ndinu wabwino pochita chisoni kuposa a chisoni onse.”

    Verse 110

    Koma inu munali kuwanyogodola mpaka pamene inu mudandiiwala Ine ndipo inu munali kuwaseka iwo

    Verse 111

    Ndithudi lero Ine ndawalipira chifukwa cha kupirira kwawo ndipo iwo ndi amene apambana

    Verse 112

    Ndipo Iye adzafunsa kuti, “Kodi inu munakhala padziko lapansi zaka zingati?”

    Verse 113

    Iwo adzayankha kuti, “Takhala tsiku limodzi kapena mphindi zochepa zokha. Afunseni iwo amene amasunga chiwerengero.”

    Verse 114

    Iye adzawayankha kuti, “Inu mukadadziwa ndi nthawi yochepa kwambiri imene inu munakhala.”

    Verse 115

    “Kodi inu mumaganiza kuti tidangokulengani inu opanda cholinga ndipo kuti simudzabwerera kwa Ife?”

    Verse 116

    Motero alemekezeke Mulungu, Mfumu ya chilungamo. Palibe Mulungu wina koma Iye yekha, Ambuye wa Mpando wolemekezeka ndi Wachifumu

    Verse 117

    Aliyense amene apembedza mulungu wina woonjezera pa Mulungu, pamene Iye alibe umboni wa chimenecho, Ambuye wake adzamufunsa. Ndithudi anthu osakhulupirira sadzapambana ayi

    Verse 118

    Nena, “Ambuye wanga! Ndikhululukireni machimo anga ndipo mundichitire chisoni chifukwa Inu ndinu wachisoni choposa a chisoni onse.”