Back to Languages

    Chichewa - Chapter 26

    Translation by Al Haji Yusuf Muhammad Kanyamula

    Verse 1

    Ta Sin Mim

    Verse 2

    Awa ndi mawu omveka a Buku la Korani

    Verse 3

    Iwe mwina ukhoza kudziononga ndi madandaulo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo

    Verse 4

    Ngati Ife tifuna, tikhoza kuwavumbulutsira chizindikiro chochokera kumwamba chimene makosi awo adzakhota modzichepetsa

    Verse 5

    Palibe chenjezo latsopano limene limadza kuchokera kwa Mwini chisoni chosatha koma iwo amalikana

    Verse 6

    Ndithudi iwo amakana mawu a Mulungu koma nkhani zidzadza kwa iwo zokhudza zinthu zimene iwo amazichita chipongwe

    Verse 7

    Kodi iwo saona nthaka, mmene ife tameretsamo mbewu zabwino zosiyanasiyana

    Verse 8

    Ndithudi m’menemu muli chizindikiro komabe ambiri a iwo sakhulupirira ayi

    Verse 9

    Ndithudi Ambuye wako ndiye Mwini mphamvu zonse ndiponso Mwini chisoni chosatha

    Verse 10

    Ndipo pamene Ambuye wako adamuitana Mose adanena kuti, “Pita kwa anthu opanda chilungamo.”

    Verse 11

    Kodi anthu a Farawo sangaope

    Verse 12

    Iye adati, “Ambuye wanga! Ndithudi ine ndili kuopa kuti adzandikana.”

    Verse 13

    “Ndipondikhozakupsamtimandikulepherakuyankhula. Tumizani Aroni.”

    Verse 14

    “Ndipo iwo ali ndi mangawa ndi ine ndipo ndichita mantha kuti akhoza kukandipha.”

    Verse 15

    Mulungu adati, “Nkosatheka kutero! Kotero pitani nonse awiri ndi zizindikiro zathu. Ife tidzakhala ndi inu ndipo tidzamva.”

    Verse 16

    Ndipo mukakafika kwa Farawo mukamuuze kuti, “Ife ndife Atumwi ochokera kwa Ambuye wa zolengedwa zonse.”

    Verse 17

    “Motero alekeni ana a Israyeli kuti apite ndi ife.”

    Verse 18

    (Farawo) adati, “Kodi ife sitidakurere iwe pamene udali wamng’ono? Ndipo iwe unakhala pakati pathu zaka zambiri.”

    Verse 19

    “Ndipo iwe udachita chimene udachita. Ndithudi iwe ndiwe mmodzi wa anthu osathokoza.”

    Verse 20

    (Mose) adati, “Ine ndidachita chimenecho popeza nthawi imeneyo ndidali wosadziwa china chilichonse.”

    Verse 21

    “Motero ine ndidathawa inu nonse pa nthawi imene ndidakuopani koma tsopano Ambuye wanga wandipatsa luntha ndiponso wandipanga ine kukhala mmodzi mwa Atumwi ake.”

    Verse 22

    “Ndipo uwu ndi mwayi umene ubwino wake iwe uli kundinyogodola. Iwe wasandutsa ana a Israyeli kukhala akapolo ako.”

    Verse 23

    Farawo adati, “Kodi Ambuye wa zolengedwa zonse ndani?”

    Verse 24

    (Mose) adati, “Ambuye wa kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zimene zili pakati pawo ngati inu mufuna kukhulupirira.”

    Verse 25

    (Farawo) adawafunsa anthu amene adamuzungulira! “Kodi muli kumva zimene ali kunenazi.”

    Verse 26

    (Mose) adapitiriza kuti, “Ambuye wanu ndiponso Ambuye wa makolo anu akale.”

    Verse 27

    (Farawo) adati, “Ndithudi Mtumwi amene watumizidwa kwa inu ndi wopenga.”

    Verse 28

    (Mose) adati, “Iye ndi Ambuye wa kum’mawa ndi kumadzulo ndi zonse zimene zikhala kumeneko ngati muli ozindikira.”

    Verse 29

    (Farawo) adayankha kuti, “Ngati iwe utumikira mulungu wina kupatula ine, ndithudi ndikupanga kukhala mmodzi wa anthu okhala ku ndende.”

    Verse 30

    (Mose) adafunsa kuti, “Kodi zingakhale choncho ngakhale nditakulangiza chizindikiro choonekeratu? “

    Verse 31

    (Farawo) adati, “Tilangize chizindikiro chako ngati zonse zimene unena ndi zoona.”

    Verse 32

    Motero Mose adaponya ndodo yake pansi ndipo nthawi yomweyo idasanduka njoka yeniyeni

    Verse 33

    Ndipo Iye adatulutsa dzanja lake ndipo nthawi yomweyo lidasanduka loyera kwa iwo amene adaliona

    Verse 34

    Farawo adauza nduna zake kuti, “Ndithudi munthu uyu ndi wodziwa matsenga.”

    Verse 35

    “Iyeyu afuna kukuchotsani m’dziko lanu ndi matsenga ake. Kodi ulangizi wanu ndi wotani ndipo ukupereka langizo lanji?”

    Verse 36

    Iwo adati, “Muyambe mwawasunga iye pamodzi ndi m’bale wake kwa kanthawi kochepa. Tumizani mithenga ku mizinda yanu

    Verse 37

    Abweretse kwa inu munthu aliyense yemwe ndi wodziwa matsenga kwambiri.”

    Verse 38

    Motero anthu amatsengawa adasonkhanitsidwa patsiku lodziwika lomwe adagwirizana

    Verse 39

    Ndipo anthu adafunsidwa kuti, “Kodi nonse mudzasonkhana?”

    Verse 40

    “Kuti mwina ife tikhoza kudzatsatira a matsenga ngati iwo atapambana.”

    Verse 41

    Ndipo pamene anthu onse amatsenga adadza kwa Farawo, iwo adati kwa Farawo, “Kodi mudzatilipira ngati titapambana?”

    Verse 42

    Iye adati, “Inde. Ndipo ndithudi inu mudzakhala kufupi ndi Ine.”

    Verse 43

    Mose adawauza kuti, “Ponyani pansi chilichonse chimene mufuna kuponya.”

    Verse 44

    Ndipo iwo adaponya zingwe ndi ndodo zawo ndipo adati: “Mwa mphamvu ya Farawo, ndithudi, ife tipambana.”

    Verse 45

    Ndipo Mose adaponya ndodo yake ndipo nthawi yomweyo idameza zonse zabodza zimene iwo adapanga

    Verse 46

    Ndipo anthu amatsenga onse aja adagwa pansi mogwada

    Verse 47

    Iwo adati, “Ife takhulupirira mwa Ambuye wa zolengedwa zonse.”

    Verse 48

    “Ambuye wa Mose ndi Aroni”

    Verse 49

    Farawo adati, “Kodi inu mwakhulupirira mwa iye pamene ine sindinakupatseni chilolezo? Ndithudi iye ndi mtsogoleri wanu amene adakuphunzitsani matsenga. Ndithudi posachedwapa mudzazindikira. Ndithudi ine ndidzadula manja anu ndi miyendo yanu moisiyanitsa. Ndidzakudulani dzanja lamanja ndi mwendo wamanzere ndiponso ndidzakupachikani pa mtanda.”

    Verse 50

    Iwo adati, “Zilibe kanthu chifukwa ndithudi ife tidzabwerera kwa Ambuye wathu.”

    Verse 51

    “Ndithudi Ife tili ndi chiyembekezo kuti Ambuye wathu adzatikhululukira machimo athu popeza ndife oyamba kukhulupirira.”

    Verse 52

    Ndipo tidamulamula Mose kuti, “Nyamuka nthawi ya usiku ndi akapolo anga chifukwa, ndithudi, inu mulondoledwa ndi gulu la adani anu.”

    Verse 53

    Ndipo Farawo adatumiza mithenga ku mizinda yonse

    Verse 54

    “Ndithudi anthu amenewa ndi kagulu ka anthu ochepa.”

    Verse 55

    “Ndithudi anthu amenewa atipsetsa mtima.”

    Verse 56

    “Ife tonse tili tcheru.”

    Verse 57

    Ndipo tidawachotsa m’minda ndi mu a kasupe

    Verse 58

    Ndiponso m’chuma ndi m’malo alionse olemekezeka

    Verse 59

    Kotero tidawapanga ana a Israyeli kukhala alowa m’malo a zinthu za anthu a Farawo

    Verse 60

    Pamene dzuwa linali kutuluka, iwo adalondoledwa ndi adani awo

    Verse 61

    Ndipo pamene magulu awiriwa adaonana wina ndi mnzake, anthu a Mose adati, “Ndithudi atipeza.”

    Verse 62

    Mose adati, “Iyayi. Ndithudi Ambuye wanga ali ndi ine ndipo adzanditsogolera.”

    Verse 63

    Ndipo tidalamulira Mose kuti, “Menya madzi a m’nyanja ndi ndodo yako.” Ndipo nyanja idagawanika pakati, mbali iliyonse idali ngati phiri lalikulu

    Verse 64

    Ndipo anthu a Farawo tidawayandikitsa ndi nyanja ija

    Verse 65

    Ndipo Ife tidapulumutsa Mose ndi onse amene adali ndi iye

    Verse 66

    Ndipo tidamiza ena

    Verse 67

    Ndithudi mu ichi muli phunziro komabe anthu ambiri sakhulupirira ayi

    Verse 68

    Ndithudi Ambuye wako! Iye ndiye Mwini mphamvu zonse ndi Mwini chisoni chosatha

    Verse 69

    Ndipo afotokozere nkhani za Abrahamu

    Verse 70

    Pamenepo iye adanena kwa abambo ake ndiponso kwa anthu ake kuti, “Kodi ndi chiyani chimene inu muli kupembedza?”

    Verse 71

    Iwo adati, “Timatumikira mafano ndipo timapempha kwa iwo modzipereka kwambiri.”

    Verse 72

    Ndipo adati, “Kodi iwo amakumvani pamene mumawapempha?”

    Verse 73

    “Kodi amakuthandizani kapena kukuonongani?”

    Verse 74

    Iwo adati, “Iyayi. Koma ife tidawapeza makolo athu akupembedza mafano.”

    Verse 75

    Iye adati, “Kodi inu muli kuzidziwa zimene muli kuzipembedza?”

    Verse 76

    “Inu ndiponso makolo anu akale?”

    Verse 77

    “Ndithudi onse ndi adani anga kupatula Ambuye wachilengedwe.”

    Verse 78

    “Amene adandipanga ine ndipo ndiye amene amandipatsa chilangizo.”

    Verse 79

    “Ndipo ndiye amene amandipatsa chakudya ndi chakumwa.”

    Verse 80

    “Ndipo ndikadwala, ndi Iye amene amandichiza.”

    Verse 81

    “Ndipo ndiye amene adzandipangitsa kuti ndife ndi kudzandibwezeranso moyo.”

    Verse 82

    “Ndi amene ine ndimayembekezera kuti adzandikhululukira machimo anga pa tsiku lachiweruzo”

    Verse 83

    Ambuye ndipatseni luntha ndipo mundilole kuti ndikhale pakati pa anthu ochita zabwino

    Verse 84

    Ndipatseni ulemerero umene udzatchulidwe ndi mibadwo yomwe ikubwera mtsogolo

    Verse 85

    Ndipo ndiikeni m’gulu la anthu amene adzakhala kumalo a mtendere a ku Paradiso

    Verse 86

    Akhululukireni abambo anga ndithudi iwo ali mmodzi mwa anthu osochera

    Verse 87

    Musadzandichititse manyazi patsiku limene anthu adzaukitsidwa kwa akufa

    Verse 88

    Tsiku limene chuma ndi ana sizidzathandiza wina aliyense

    Verse 89

    Kupatula yekhayo amene adzadza kwa Mulungu ndi mtima woyera

    Verse 90

    Pamenepo Paradiso idzayandikiritsidwa kwa anthu angwiro

    Verse 91

    Ndipo Gahena idzaonetsedwa poyera kwa anthu ochimwa

    Verse 92

    Mawu adzanenedwa kwa iwo kuti, “Kodi mafano anu aja amene mumatumikira ali kuti?”

    Verse 93

    Kuwonjezera pa Mulungu weniweni? Kodi iwo akhoza kukuthandizani inu kapena kudzithandiza okha?”

    Verse 94

    Ndipo iwo ndi onse ochimwa adzaponyedwa ku Gahena

    Verse 95

    Ndiponso pamodzi ndi magulu onse a Satana

    Verse 96

    Iwo adzati pamene adzakhala ali kukangana kumeneko

    Verse 97

    “Pali Mulungu, ndithudi, ife tidali ochimwa moonekeratu.”

    Verse 98

    Pamene tidakusandutsani inu kukhala ofanana ndi Ambuye wa zolengedwa zonse

    Verse 99

    Palibe ena koma anthu ochita zoipa amene adatisocheretsa ife

    Verse 100

    Palibe wina woti angatipepesere ife

    Verse 101

    Ndiponso palibe bwenzi lenileni

    Verse 102

    Koma tikadakhalanso ndi moyo, tikadakhala anthu okhulupirira

    Verse 103

    Ndithudi mu zimenezi muli chizindikiro koma anthu ambiri sakhulupirira ayi

    Verse 104

    Ndithudi Ambuye wanu! Ndiye Mwini mphamvu zonse ndi Mwini chisoni chosatha

    Verse 105

    Anthu a m’badwo wa Nowa adakana Atumwi awo

    Verse 106

    Pamene Nowa adati, “Kodi inu simungaope Mulungu ndi kumumvera Iye?”

    Verse 107

    “Ndithudi ine ndine Mtumwi wanu wokhulupirika.”

    Verse 108

    “Motero opani Mulungu ndipo mundimvere ine.”

    Verse 109

    “Ine sindikupemphani malipiro ena alionse chifukwa palibe wina aliyense amene angandilipire ine kupatula Ambuye wa zolengedwa zonse.”

    Verse 110

    “Kotero opani Mulungu ndipo mundimvere ine.”

    Verse 111

    Iwo adati, “Kodi ife tikukhulupirire iwe pamene anthu onyozeka ndiwo amene amakutsatira iwe?”

    Verse 112

    Nowa adati, “Kodi ine ndikudziwa chiyani za chimene iwo amachita?”

    Verse 113

    “Ambuye wanga ndiye amene akhoza kuweruza ngati mumazindikira.”

    Verse 114

    “Ndipo ine sindidzathamangitsa anthu okhulupirira moona.”

    Verse 115

    “Ine ndine wopereka chenjezo poyera.”

    Verse 116

    Iwo adati, “Iwe Nowa; ngati siusiya zimene uchita udzaponyedwa miyala.”

    Verse 117

    Iye adati, “Ambuye wanga! Ndithudi anthu anga akundikana.”

    Verse 118

    Motero weruzani mwachilungamo pakati pa ine ndi iwo. Ndipulumutseni ine pamodzi ndi anthu okhulupirira amene ali ndi ine

    Verse 119

    Ife tidamupulumutsa iye pamodzi ndi iwo amene adali naye m’chombo

    Verse 120

    Ndipo pambuyo pake tidamiza ena onse ndi chigumula

    Verse 121

    Ndithudi mu chimenechi muli phunziro komabe ambiri sakhulupirira

    Verse 122

    Ndithudi Ambuye wako ndi Mwini mphamvu ndi Mwini chisoni chosatha

    Verse 123

    Anthu a ku Aad sanakhulupirire Atumwi awo

    Verse 124

    Pamene m’bale wawo Houd adati, “Kodi inu simungakhale ndi mantha ndi Mulungu?”

    Verse 125

    “Ndithudi ine ndine Mtumwi wanu wokhulupirika.”

    Verse 126

    “opani Mulungu ndipo munditsate ine.”

    Verse 127

    “Pa ntchito iyi, ine sindipempha malipiro kuchokera kwa inu chifukwa palibe wina amene angandilipire kupatula Ambuye wa zolengedwa zonse.”

    Verse 128

    “Kodi inu mukumamanga nyumba pamalo paliponse pokwera mofuna kudzisangalatsa?”

    Verse 129

    “Kodi muli kumanga nyumba zokongola ndi zolimba ngati kuti mudzakhalamo mpaka kalekale?”

    Verse 130

    “Ndipo pamene mumenya anthu mumamenya ngati anthu ankhanza.”

    Verse 131

    “Motero opani Mulungu, ndipo mundimvere ine.”

    Verse 132

    “Ndipo muopeni Iye amene wakupatsani inu zinthu zonse zimene mumazidziwa.”

    Verse 133

    “Iye wakupatsani nyama ndi ana,”

    Verse 134

    “Ndiponso minda ndi a kasupe;”

    Verse 135

    “Ndithudi ine ndili kuchita mantha ndi chilango chimene chidzadza pa inu pa tsiku loopsa.”

    Verse 136

    Iwo adati, “Ndi chimodzimodzi kwa ife kaya utilalikira kapena ayi.”

    Verse 137

    “Zonse zimene uli kutiopseza nazo ndi chikhalidwe cha anthu amakedzana.”

    Verse 138

    “Ife sitidzalangidwa ayi.”

    Verse 139

    Iwo adamukana iye ndipo Ife tidawaononga onse. Ndithudi mu chimenechi muli phunziro koma ambiri sakhulupirira ayi

    Verse 140

    Ndithudi Ambuye wako ndiye Mwini mphamvu zonse ndi Mwini chisoni chosatha

    Verse 141

    Anthu a Thamoud adakana Atumwi awo

    Verse 142

    Pamene m’bale wawo Saleh adati, “Kodi inu simungakhale ndi mantha ndi Mulungu?”

    Verse 143

    “Ndithudi ine ndine Mtumwi wanu okhulupirika.”

    Verse 144

    “Motero opani Mulungu ndipo mundimvere ine.”

    Verse 145

    “Pa ntchito iyi ine sindili kukupemphani malipiro. Palibe wina amene angandilipire kupatula Ambuye wa zolengedwa zonse.”

    Verse 146

    “Kodi inu muganiza kuti mudzasiyidwa mu mtendere wa m’dziko lino?”

    Verse 147

    “M’kati mwa minda ndi a kasupe.”

    Verse 148

    “Minda ya chimanga ndi mitengo ya tende imene yapatsa zipatso zambiri.”

    Verse 149

    “Ndipo muboola mapiri ndi kumangamo nyumba zanu mwaukatswiri;”

    Verse 150

    “Khalani ndi mantha ndi Mulungu ndipo mundimvere ine.”

    Verse 151

    “Musamvere malamulo a anthu oononga.”

    Verse 152

    “Amene amachita zoipa padziko lapansi ndipo sakonza makhalidwe awo.”

    Verse 153

    Iwo adati, “Iwe uli mmodzi mwa olodzedwa.”

    Verse 154

    “Iwe ndiwe munthu wonga ife tomwe. Tilangize chizindikiro ngati zimene ukunenazi ndi zoona”

    Verse 155

    Iye adati, “Iyi ndi ngamira yaikazi. Iyo idzamwa madzi patsiku lake ndipo inu mudzamwa patsiku lanu lokhazikitsidwa.”

    Verse 156

    “Musaizunze ayi chifukwa mukatero chilango cha tsiku loopsa chidzadza kwa inu.”

    Verse 157

    Komabe iwo adaipha iyo ndipo adanong’oneza bombono

    Verse 158

    Chilango chidawapeza iwo. Ndithudi mu chimenechi muli chizindikiro koma ambiri a iwo sakhulupirira

    Verse 159

    Ndithudi Ambuye wako! Indedi ndiye Mwini mphamvu zonse ndi Mwini chisoni chosatha

    Verse 160

    Anthu a Loti adakana Atumwi awo

    Verse 161

    Pamene m’bale wawo Loti adati, “Kodi inu simungaope Mulungu?”

    Verse 162

    “Ndithudi ine ndine Mtumwi wanu wokhulupirika.”

    Verse 163

    “Opani Mulungu ndipo mundimvere ine.”

    Verse 164

    “Ine sindili kupempha kuti mundilipire chifukwa cha ichi ayi chifukwa palibe wina amene angandilipire kupatula Ambuye wa zolengedwa zonse.”

    Verse 165

    “Kodi inu mwasankha kuti muzigonana ndi amuna anzanu mwa zolengedwa zonse

    Verse 166

    “Kusiya akazi amene Mulungu adakulengerani? Koma inu ndinu anthu olakwa kwambiri.”

    Verse 167

    Iwo adati, “Iwe Loti! Ngati siusiya zimenezi ndithudi udzakhala mmodzi mwa othamangitsidwa.”

    Verse 168

    Iye adati, “Ine ndili kudana ndi makhalidwe anu.”

    Verse 169

    “Ambuye wanga! Ndipulumutseni ine pamodzi ndi a pabanja langa ku ntchito zawo zoipa.”

    Verse 170

    Ndipo Ife tidamupulumutsa iye pamodzi ndi anthu ake onse

    Verse 171

    Kupatula mayi wokalamba, pakati pa amene adatsalira m’mbuyo

    Verse 172

    Ndipo Ife tidawaononga kwambiri ena onse

    Verse 173

    Ndipo choipa chidali chilango cha mvula imene idagwa pa iwo amene adachenjezedwa koma sadamvere

    Verse 174

    Ndithudi mu ichi muli phunziro koma ambiri a iwo sakhulupirira

    Verse 175

    Ndithudi Ambuye wako ndiye mwini mphamvu zonse ndi mwini chisoni chosatha

    Verse 176

    Nawonso anthu okhala m’nkhalango adakana Atumwi

    Verse 177

    Pamene Shaibu adawauza kuti, “Kodi inu simungaope Mulungu?”

    Verse 178

    “Ndithudi ine ndine Mtumwi wanu wokhulupirira.”

    Verse 179

    “Opani Mulungu ndipo mundimvere ine.”

    Verse 180

    “Ine sindikupemphani malipiro chifukwa palibe wina aliyense amene angandilipire kupatula Ambuye wa zolengedwa zonse.”

    Verse 181

    “Perekani muyeso oyenera ndipo musachepetse.”

    Verse 182

    “Yesani ndi miyeso yabwino.”

    Verse 183

    “Ndipo musawachepetsere anthu zinthu zawo kapena kulowetsa chisokonezo m’dziko.”

    Verse 184

    “Muopeni Iye amene adakulengani inu ndi mibadwo yakale.”

    Verse 185

    Iwo adati, “Ndithudi iwe walodzedwa.”

    Verse 186

    “Iwe ndiwe munthu wolingana ndi ife. Ndithudi ife tili kuganiza kuti iwe uli kunama.”

    Verse 187

    “Tigwetsere mtambo kuchokera kumwamba ngati zimene uli kunena ndi zoonadi.”

    Verse 188

    Iye adati, “Ambuye wanga amadziwa kwambiri chimene inu mumachita.”

    Verse 189

    Iwo adamukana iye kotero chilango cha thambo ndi moto chidawaononga. Ichi chidali chilango cha tsiku loopsa

    Verse 190

    Ndithudi mu chimenechi muli chiphunzitso koma ambiri a iwo sakhulupirira

    Verse 191

    Ndithudi Ambuye wako ndiye Mwini mphamvu zonse ndi Mwini chisoni chosatha

    Verse 192

    Buku lolemekezekali lavumbulutsidwa ndi Ambuye wa zolengedwa zonse

    Verse 193

    Mzimu wokhulupirika udabweretsa Bukuli

    Verse 194

    Ku mtima wako kuti ukhoza kuchenjeza mitundu ya anthu

    Verse 195

    Mu chinenero chomveka cha Chiarabu

    Verse 196

    Ndithudi lili kupezeka mu mawu a Mulungu akale

    Verse 197

    Kodi si chizindikiro kwa iwo kuti anthu ophunzira a ana a Israyeli amalidziwa

    Verse 198

    Ngati Ife tikadaivumbulutsa kwa munthu wa mtundu wina uliwonse yemwesi wa Chiarabu

    Verse 199

    Kuti iye ailakatule kwa iwo ndipo sakadakhulupirira iwo mwa Bukulo

    Verse 200

    Kotero Ife tidaipanga iyo kuti ilowe m’mitima ya anthu ochitazoipa

    Verse 201

    Iwosadzakhulupiriramuilompakapamene adzaona chilango chowawa

    Verse 202

    Ndipo icho chidzadza kwa iwo mwadzidzidzi pamene iwo sakudziwa

    Verse 203

    Ndipo iwo adzati, “Kodi ife sitidzapatsidwanso nthawi?”

    Verse 204

    Kodi iwo angafune kuti chilango chathu chidze msanga

    Verse 205

    Tandiuza. Ngati Ife titawalola kukhala mu mtendere wa zaka zambiri

    Verse 206

    Ndipo pambuyo pake chilango chimene chidalonjezedwa chidza pa iwo

    Verse 207

    Chisangalalo chawo chimene adapatsidwa chidzakhala chopanda phindu

    Verse 208

    Palibe mtundu wa anthu umene tidaonongapo kale umene sitidautumizire owachenjeza

    Verse 209

    Monga chenjezo ndipo Ife si ndife opondereza ayi

    Verse 210

    Si a Satana amene adabweretsa Korani ino ayi

    Verse 211

    Si koyenera kwa iwo ndiponso sangathe kutero

    Verse 212

    Ndithudi iwo amanidwa kumva za Bukuli

    Verse 213

    Musapembedze milungu ina kuonjezera pa Mulungu weniweni chifukwa mukatero mudzakhala m’gulu limene lidzalangidwa

    Verse 214

    Achenjeze abale ako amene ali pafupi ndi iwe

    Verse 215

    Ndipo onetsa chifundo kwa anthu okhulupirira amene amakutsatira iwe

    Verse 216

    Ngati iwo sakumvera iwe, unene kuti, “Ine sindidzaimbidwa mlandu chifukwa cha zimene mumachita.”

    Verse 217

    Ika chikhulupiriro chako mwa Mwini mphamvu zonse ndi Mwini chisoni chosatha

    Verse 218

    Amene amakuona pamene umaimirira popemphera

    Verse 219

    Ndi machitidwe ako pakati pa anthu opemphera

    Verse 220

    Mulungu amamva chilichonse ndipo amadziwa china chilichonse

    Verse 221

    Kodi ndi kuuzeni za munthu amene Satana amamutsikira

    Verse 222

    Iwo amadza pa munthu wabodza ndi wochimwa

    Verse 223

    Iwo amamvera mabodza okhaokha ndipo komaambiriaiwondiabodza

    Verse 224

    Alakatuliamatsatidwandi anthu ochita zoipa

    Verse 225

    Kodi simuona kuti iwo amangonena nkhani iliyonse mu zolakatula zawo

    Verse 226

    Ndipo iwo amakamba zinthu zimene iwo sachita

    Verse 227

    Kupatula okhawo amene akhulupirira ndipo amachita ntchito zabwino ndi kumakumbukira Mulungu kwambiri ndi kudziteteza pambuyo pa kuponderezedwa. Ndipo iwo amene amachita zoipa adzadziwa chimene chidzawagadabuza