Back to Languages
Chichewa - Chapter 81
Translation by Al Haji Yusuf Muhammad Kanyamula
Verse 1
Pamene dzuwa lidzavundikiridwa
Verse 2
Ndi pamene nyenyezi zidzagwa pansi
Verse 3
Ndi pamene mapiri adzachotsedwa
Verse 4
Ndi pamene ngamila zabele zizakhala zosasamalidwa
Verse 5
Ndi nyama za m’tchire zidzasonkhanitsidwa pamodzi
Verse 6
Ndi pamene nyanja zidzayatsidwa moto kapena zidzasefukira
Verse 7
Ndi pamene mizimu idzakumanitsidwa ndi matupi awo
Verse 8
Ndi pamene mwana wa mkazi wa mng’ono, amene adaundilidwa wa moyo adzafunsidwa
Verse 9
Chifukwa chimene anamuphera
Verse 10
Ndi pamene mabuku olembamo ntchito za munthu aliyense adzatulutsidwa
Verse 11
Ndi pamene kumwamba kudzafafanizidwa ndi kuchotsedwa ku malo ake
Verse 12
Ndi pamene Gahena idzatenthetsedwa kwambiri
Verse 13
Ndi pamene Paradiso idzafikitsidwa pafupi
Verse 14
Ndithudi munthu aliyense adzadziwa chimene adachita
Verse 15
Motero, ndithudi, Ine ndili kulumbira pali nyenyezi zimene zimalowa
Verse 16
Ndi pali maiko zimene zimayenda mofulumira ndi kudzibisa okha
Verse 17
Ndi pali usiku pamene uchoka
Verse 18
Ndipalim’mawapamenekulikucha
Verse 19
Ndithudi awa ndi Mau a Mtumwi wolemekezeka
Verse 20
Mwini mphamvu amene amalemekezedwa ndi Ambuye, Mwini Mpando wa Chifumu
Verse 21
Amamveredwa ndi wokhulupirika
Verse 22
Ndipo m’bale wanu uyu si wa misala ayi
Verse 23
Ndipo, ndithudi, iye adamuona iye mu mlengalenga
Verse 24
Iye sabisa zinthu zosaoneka
Verse 25
Ndipo zimene alankhula sizochokera kwa Satana wotembereredwa
Verse 26
Kodi inu muli kupita kuti
Verse 27
Ndithudi ichi si china chilichonse ayi koma chikumbutso kwa anthu a mitundu yonse
Verse 28
Kwa aliyense wa inu amene afuna kuyenda moongoka
Verse 29
Koma inu simungathe kutero pokhapokha ndi chifuniro cha Mulungu, Ambuye wa zolengedwe zonse