Back to Languages

    Chichewa - Chapter 93

    Translation by Al Haji Yusuf Muhammad Kanyamula

    Verse 1

    Pali usana

    Verse 2

    Ndi pali usiku pamene ulipo

    Verse 3

    Ambuye wako sadakutaye iwe ndiponso sakudana nawe ayi

    Verse 4

    Ndipo, ndithudi, moyo umene uli nkudza ndi wabwino kwa iwe kuposa moyo uno

    Verse 5

    Ndithudi Ambuye wako adzakupatsa, ndipo iwe chidzakukondweretsa

    Verse 6

    Kodi sadakupeze iwe uli wa masiye ndipo adakupatsa malo okhala

    Verse 7

    Kodi sadakupeze uli wosochera ndipo Iye adakutsogolera

    Verse 8

    Kodi sadakupeze iwe waumphawi ndipo adakulemeretsa

    Verse 9

    Motero iwe usapondereze pansi mwana wa masiye

    Verse 10

    Ndipo usapirikitse munthu wopempha

    Verse 11

    Koma lengeza chisomo cha a Ambuye wako